Vumbulutso loperekedwa kudzera mwa Joseph Smith Mneneri kwa Sidney Rigdon, Parley P. Pratt, ndi Leman Copley, ku Kirtland, Ohio, Meyi 7, 1831. Leman Copley adali atalandira uthenga wabwino koma adakakamirabe ku ziphunzitso zina za gulu la Shakers (United Society of Believers in Christ’s Second Appearing), limene iye adali nalo poyamba. Zina mwa zikhulupiliro za a Shakers zidali zakuti Kudza Kwachiwiri kwa Khristu kudali kutachitika kale komanso kuti Iye adaonekera mu maonekedwe a mkazi, Ann Lee. Iwo sankaona ubatizo wa m’madzi kukhala wofunikira. Iwo amakana ukwati ndipo amakhulupilira moyo wa umbeta kotheratu. Ma Shakers ena amaletsanso kudya nyama. Mu kutsogoza vumbulutsoli, mbiri ya Joseph Smith ikuti, “Kuti tikhale ndi kumvetsetsa kokwanira pa nkhaniyi, ndidafunsa kwa Ambuye, ndipo ndidalandira zotsatirazi.” Vumbulutsoli limatsutsa mfundo zina zofunikira za gulu la Shaker. Abale amene tawatchulawo adatenga kope la vumbulutsoli ku gulu la Shaker (pafupi ndi Cleveland, Ohio) ndi kuliwerenga lonse kwa iwo, koma ilo lidakanidwa.