Vumbulutso la kakhazikitsidwe ndi kayendetsedwe ka Mpingo, loperekedwa kudzera kwa Joseph Smith Mneneri, ku kapena pafupi ndi Fayette, New York. Magawo a vumbulutsoli atha kukhala kuti adaperekedwa cha m’chirimwe cha 1829. Vumbulutso lathunthu, lodziwika pa nthawiyo ngati Mfundo ndi Mapangano, n’kutheka kuti lidalembedwa patangotha Epulo 6, 1830 (tsiku limene Mpingo udakhazikitsidwa). Mneneri adalemba, “Tidalandira kwa Iye [Yesu Khristu] zotsatirazi, mwa mzimu wa uneneri ndi vumbulutso; zimene sizidangotipatsa ife chidziwitso chochuluka, komanso zidasonyeza kwa ife tsiku lenileni limene, molingana ndi chifuniro Chake ndi lamulo, tikuyenera kupitiriza kukhazikitsanso Mpingo Wake pano pa dziko lapansi,”