1–10, Akulu akuitanidwa kukalalikira uthenga wabwino, kubatiza wotembenuka, ndi kumanga Mpingo; 11–12, Iwo akuyenera kuitanidwa ndi kudzodzedwa ndipo akuyenera kuphunzitsa mfundo za uthenga wabwino opezeka m’malembo oyera; 13–17, Iwo akuyenera kuphunzitsa ndi kunenera ndi mphamvu ya Mzimu; 18–19, Oyera Mtima akulamulidwa kuti asaphe, asabe, asaname, asasilire, asachite chigololo, kapena kuyankhula zoipa kwa wina ndi mzake; 30–39, Malamulo otsogolera kupereka chuma akhazikitsidwa; 40–42, Kudzikweza ndi ulesi zidzudzulidwa; 43–52, Odwala akuyenera kuchiritsidwa kudzera mu kutumikiridwa ndi mwa chikhulupiliro; 53–60, Malemba Oyera amatsogolera Mpingo ndipo akuyenera kulengezedwa ku dziko; 61–69, Malo a Yerusalemu Watsopano ndi zinsinsi za ufumu zidzavumbulutsidwa; 70–73, Chuma choperekedwa chikuyenera kugwiritsidwa pothandizira adindo a Mpingo; 74–93, Malamulo otsogolera za chigololo, zadama, kupha, kuba,ndi kuwulura kwa machimo akhazikitsidwa.