1–5, Oyera mtima okhulupirika amalandira Mtonthozi ameneyo, amene ali lonjezo la moyo wosatha; 6–13, Zinthu zonse zimalamulidwa ndi kulamuliridwa ndi Kuwala kwa Khristu; 14–16, Chiukitso chimadza kudzera mu Chiwombolo; 17–31, Kumvera ku lamulo la selestiyo, la terestriyo, kapena la telestiyo kumakonzekeretsa anthu ku maufumu ndi ulemererowo; 32–35, Awo amene akufuna kukhala mu uchimo akhalabe anyansi; 36–41, Maufumu onse amalamulidwa ndi chilamulo; 42–45, Mulungu adapereka lamulo kwa zinthu zonse; 46–50, Munthu adzazindikira ngakhale Mulungu; 51–61, Fanizo la munthu wotumiza antchito ake kumunda ndi kuwayendera iwo motsatira; 62–73, Yandikirani kwa Ambuye, ndipo mudzaona nkhope Yake; 74–80, Dziyeretseni nokha ndi kuphunzitsana wina ndi mzake ziphunzitso za ufumu; 81–85, Munthu aliyense amene wachenjezedwa akuyenera kuchenjeza mnansi wake; 86–94, Zizindikiro, kugwedezeka kwa chilengedwe, ndi angelo amakonza njira ya kudza kwa Ambuye; 95–102, Malipenga aungelo amaitana akufa mu dongosolo lawo; 103–116, Malipenga a angelo alengeza za chibwenzeretso cha uthenga wabwino, kugwa kwa Babulo, ndi nkhondo ya Mulungu wamkulu; 117–126, Funani maphunziro, khazikitsani nyumba ya Mulungu (kachisi), ndipo mudziveke nokha ndi chomangira cha chikondi; 127–141, Dongosolo la Sukulu ya Aneneri ikhazikitsidwa, kuphatikizapo mwambo wa kusambitsa mapazi.