Malembo Oyera
Chiphunzitso ndi Mapangano 40


Gawo 40

Vumbulutso loperekedwa kwa Joseph Smith Mneneri ndi Sidney Rigdon, ku Fayette, New York, January 6, 1831. Kutsogola zolemba za vumbulutsoli, mbiri ya Mneneri ikuti, “Monga James [Covel] adakana mawu a Ambuye, ndikubwelera ku mfundo zake zakale ndi anthu, Ambuye adapereka kwa ine ndi Sidney Rigdon vumbulutso lotsatirali” (onani gawo 36).

1–3, Kuopa chizunzo ndi kusamalira za dziko zimayambitsa kukana uthenga wabwino.

1 Taonani, inde ine ndinena kwa inu, kuti ntima wa mtumiki wanga James Covel udali wolungama pamaso panga, pakuti adapanga pangano ndi ine kuti adzamvera mawu anga.

2 Ndipo adalandira mawuwo mokondwera, koma pomwepo adamuyesa Satana; ndipo kuopa mazunzo ndi kusamalira za dziko zidampangitsa kukana mawu.

3 Kotero adaphwanya pangano langa, ndipo zikhala ndi ine kumuchitira iye monga ndikufunira ine. Ameni.