Gawo 79
Vumbulutso loperekedwa kudzera mwa Joseph Smith Mneneri, ku Hiram, Ohio, Malitchi 12, 1832.
1–4, Jared Carter aitanidwa kukalalikira uthenga wabwino ndi Mtonthozi.
1 Indetu ndinena kwa iwe, kuti ndi chifuniro changa kuti mtumiki wanga Jared Carter apitenso ku maiko a kum’mawa, kuchokera malo ndi malo, ndi kuchokera mzinda ndi mzinda, mu mphamvu ya kudzodza kumene iye wadzodzedwera, kulengeza uthenga wabwino wa chisangalalo chachikulu, ngakhale uthenga wabwino wosatha,
2Â Ndipo ndidzatumiza pa iye Mtonthozi, amene adzamuphunzitsa iye choonadi ndi njira imene iye adzapite;
3Â Ndipo pamene iye ali wokhulupirika, ndidzamuvekanso iye korona ndi mitolo.
4Â Kotero, mtima wako ukhale okondwera, mtumiki wanga Jared Carter, ndipo usaope, atero Ambuye, ngakhale Yesu Khristu. Ameni.